06/12/2024
Mzimu oyela kumuikila malile π€π€π€π€π€π€π€
Mtsogoleri wa mpingo wa Katolika pa dziko lonse, Papa Francis, walimbikitsa alaliki kuti ulaliki wawo usamatalike kupitilira mphindi khumi.
Poyankhula Lachitatu sabata ino pa tchalitchi cha Saint Peter's Square ku Rome, Papa Francis wati nthawi zonse ulaliki umayenera kutsogozedwa ndi Mzimu Woyera, choncho kulalikira nthawi yaitali kumamuika mlalikiyo pa mayesero olalikira za m'mutu mwake osati zomwe Mzimu Woyera akunena.
Malingana ndi tsamba la Vatican News, Papa Francis wati uthenga wabwino uyenera kulalikidwa βmwa Mzimu Woyera. Kulalikira ndi kudzoza kwa Mzimu Woyera kumatanthauza kufalitsa, pamodzi ndi malingaliro ndi chiphunzitso, moyo ndi kukhudzika kwakukulu, ndipo motero osati ndi mawu a nzeru okopa, koma ndi chionetsero cha Mzimu ndi mphamvu."
Popitilira, Papa Francis wati, βPakadutsa mphindi 8, kulalikira kumabalalika ndipo palibe amene amakumvetsa. Musapitirire mphindi 10, ayi! Izi ndizofunikira kwambiri."
Iye anati, alaliki ayenera kupempherera chisomo cha Mzimu Woyera kuti alengeze Khristu mβkulalikira kwawo. Apa anatsindikaso kuti alaliki sayenera kudzilalikira okha koma Yesu Mkhilisitu.
Pakadali pano, mtsutso wakula pamasamba anchezo. Pomwe ena akugwirizana ndi zomwe Papa Francis wayankhulazi, ena akutsutsa ponena kuti Mzimu Woyera sumayenera kudulilidwa malire.